Pamene aneneri ndi aphunzitsi a tchalitchi chakale
anali kusala kudya ndi kupemphera, Mzimu Woyera unauza Paulo ndi Baranaba
kuti ayende ulendo woyamba wa umishonale.
Tchalitchi chinawapempherera asananyamuke ulendo wawowo.
Iwo anaikidwa manja, ndipo tinawapempherera mochokera pansi pa mtima.
Monga tchalitchi chogwirizana, tinawapempherera kuti ayende bwino
ndiponso kuti Mulungu awapatse mawu oyenerera
oti akayankhule kwa anthu ambirimbiri.
Tinapempherera amishonale athuwa kuti zinthu ziwayendere bwino
pantchito yawo yofalitsa uthenga wabwino.
Paulo ndi Baranaba anayenda kupita kumadera osiyanasiyana.
Ku Kupro, analalikira mawu a Mulungu m'masunagoge a Ayuda.
Ku Antiyokeya wa ku Pisidiya, pafupifupi anthu onse mumzindawo anasonkhana
kuti adzamve mawu a Ambuye.
Anthu Amitundu atamva uthenga wawo, anakhulupirira.
Mawu a Ambuye anafalikira m'chigawo chonse,
ndipo ophunzira anali kusangalala kwambiri komanso anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
Paulo ndi Baranaba anaika akulu mu tchalitchi chilichonse
ndipo ankasala kudya ndi kuwapempherera powapereka kwa Ambuye.
Iwo anasonkhanitsa tchalitchi chonse pamodzi n'kuwauza
zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwowo
ndiponso mmene anatsegulira khomo la chikhulupiriro kwa anthu Amitundu.